Marko 14:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo iye yekha adzakusonyezani cipinda ca pamwamba cacikuru coyalamo ndi cokonzedwa; ndipo m'menemo mutikonzere.

16. Ndipo ophunzira anaturuka, nafika m'mzinda, napeza monga anati kwa iwo; ndipo anakonza Paskha.

17. Ndipo pofika madzulo anadza Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.

18. Ndipo pamene anaseama iwo kudya, Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Mmodzi wa inu adzandipereka Ine, ndiye wakudya ndi Ine pamodzi.

19. Anayamba iwo kukhala ndi cisoni, ndi kunena naye mmodzi mmodzi, kuti, Ndine kodi?

20. Ndipo anati kwa iwo, Mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndiye wakusunsa pamodzi ndi Ine m'mbale.

Marko 14