Marko 13:5-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Yesu anayamba kunena nao, Yang'anirani kuti munthu asakusoceretseni.

6. Ambiri adzafika m'dzina langa, nadzanena, Ine ndine Iye; nadzasoceretsa ambiri.

7. Ndipo m'mene mudzamva za nkhondo ndi mbiri zace za nkhondo, musamadera nkhawa: ziyenerakucitika izi; koma sicinafike cimariziro.

8. Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzace: padzakhaia zibvomezi m'malo m'malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.

9. Koma inu mudziyang'anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu kwa akuru a mirandu; ndipo adzakukwapulani m'masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafwnu mudzaimirira cifukwa ca Ine, kukhale umboni kwa iwo.

10. Ndipo Uthenga Wabwino uyenera uyambe kulalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.

11. Ndipo pamene adzapita nanu kumlandu, nadzakuperekani, musada nkhawa usanayambe mrandu ndi cimene mudzalankhula; koma ci mene cidzapatsidwa kwa inu m'mphindi yomweyo, mucilankhule; pakuti olankhula si ndinu, koma Mzimu Woyera.

12. Ndipo mbale adzapereka mbale wace kuti amuphe, ndi atate mwana wace; ndi ana adza yambana ndi akuwabala, nadzawaphetsa,

13. Ndipo adzada inu anthu onse cifukwa ca dzina langa: koma iye wakupirira kufikira cimariziro, yemweyo adzapulumutsidwa.

14. Ndipo pamene mukaona conyansa ca kupululutsa cirikuima pomwe siciyenera (wakuwerenga azindikile), pamenepo a m'Yudeya athawire kumapiri;

15. ndi iye amene ali pamwamba pa chindwi asatsike, kapena asalowe kukaturutsa kanthu m'nyumba mwace;

16. ndi iye amene ali kumunda asabwere kudzatenga Malaya ace.

17. Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana masiku awol

18. Ndipo pempherani kuti kusakhale m'nyengo yacisanu.

Marko 13