Marko 12:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo iwo anamtenga iye, nampanda, namcotsa wopanda kanthu.

4. Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namcitira zomcititsa manyazi.

5. Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.

6. Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wace wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamcitira ulemu mwana wanga.

7. Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.

8. Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.

9. Pamenepo mwini munda adzacita ciani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.

Marko 12