Marko 11:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo ansembe akuru ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, cifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi ciphunzitso cace.

19. Ndipo masiku onse madzulo anaturuka Iye m'mudzi.

20. Ndipo m'mene anapitapo m'mawa mwace, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.

21. Ndipo Petro anakumbukila, nanena naye, Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.

22. Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu,

Marko 11