Marko 1:42-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Ndipo pomwepo khate linamcoka, ndipo anakonzedwa.

43. Ndipo anamuuzitsa, namturutsa pomwepo,

44. nanena naye, Ona, usati unene kanthu kwa munthu ali yense: koma muka, ukadzionetse kwa wansembe, nupereke pa makonzedwe ako 1 zimene adalamulira Mose, zikhale mboni kwa iwo.

45. Koma 2 iye anaturuka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanadziwa kulowansopoyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a ku malo onse.

Marko 1