Marko 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. CIYAMBI cace ca Uthenga Wabwino wa Yesu Kristu, Mwana wa Mulungu.

2. Monga mwalembedwa m'Yesaya mneneri,Ona, ndituma mthenga wanga patsogolo pa nkhope yanu,Amene adzakonza njira yanu;

3. Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani khwalala la Ambuye, Lungamitsani njira zace;

4. Yohane anadza nabatiza m'cipululu, nalalikira ubatizo wa kutembenuka mtima wakuloza ku cikhululukiro ca macimo.

Marko 1