Maliro 5:15-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Cimwemwe ca mtima wathu calekeka,Masewera athu asanduka maliro.

16. Korona wagwa pamutu pathu;Kalanga ife! pakuti tinacimwa.

17. Cifukwa ca ici mtima wathu ufoka,Cifukwa ca izi maso athu acita cimbuuzi;

18. Pa phiri la Ziyoni lopasukaloAnkhandwe ayendapo.

19. Inu, Yehova, mukhala cikhalire,Ndi mpando wanu wacifumu ku mibadwo mibadwo.

20. Bwanji mutiiwala ciiwalire,Ndi kutisiya masiku ambirimbiri;

21. Mutitembenuzire kwa Inu, Yehova, ndipo tidzatembenuzidwadi,Mukonzenso masiku athu ngati kale lija.

22. Koma mwatikaniza konse,Mwatikwiyira kopambana.

Maliro 5