13. Anyamata ananyamula mphero,Ana nakhumudwa posenza nkhuni.
14. Akulu adatha kuzipata,Anyamata naleka nyimbo zao.
15. Cimwemwe ca mtima wathu calekeka,Masewera athu asanduka maliro.
16. Korona wagwa pamutu pathu;Kalanga ife! pakuti tinacimwa.
17. Cifukwa ca ici mtima wathu ufoka,Cifukwa ca izi maso athu acita cimbuuzi;
18. Pa phiri la Ziyoni lopasukaloAnkhandwe ayendapo.
19. Inu, Yehova, mukhala cikhalire,Ndi mpando wanu wacifumu ku mibadwo mibadwo.
20. Bwanji mutiiwala ciiwalire,Ndi kutisiya masiku ambirimbiri;
21. Mutitembenuzire kwa Inu, Yehova, ndipo tidzatembenuzidwadi,Mukonzenso masiku athu ngati kale lija.
22. Koma mwatikaniza konse,Mwatikwiyira kopambana.