Macitidwe 9:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo poyenda ulendo wace, kunali kuti iye anayandikira Damasiko: ndipo mwadzidzidzi kudawala momzingira kuunika kocokera kumwamba;

4. ndipo anagwa pansi, namva mau akunena naye, Saulo, Saulo, Undilondalonderanji?

5. Koma anati, Ndiouyani Mbuye? Ndipo anati, Ndine Yesu amene umlondalonda;

6. komatu, uka, nulowe m'mudzi, ndipo kudzanenedwa kwa iwe cimene uyenera kucita.

7. Ndipo amunawo akumperekeza iye anaima du, atamvadi mau, koma osaona munthu.

8. Ndipo Saulo anauka; koma potseguka maso ace, sanapenya kanthu; ndipo anamgwira dzanja, namtenga nalowa naye ni'Damasiko.

Macitidwe 9