Macitidwe 7:46-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. amene anapeza cisomo pamaso pa Mulungu, napempha kuti apeze mokhalama Mulungu wa Yakobo.

47. Kama 19 Solomo anammangira nyumba.

48. Komatu 20 Wamwambamwambayo sakhala m'nyumba zomangidwa ndi manja; monga mneneri anena,

49. 21 Thambo la kumwamba ndilo mpando wacifumu wanga,Ndi dziko lapansi copondapo mapazi anga:Mudzandimangira nyumba yotani? ati Ambuye;Kapena malo a mpumulo wanga ndi otani?

50. Silinapanga dzanja langa zinthu izi zonse kodi?

Macitidwe 7