46. amene anapeza cisomo pamaso pa Mulungu, napempha kuti apeze mokhalama Mulungu wa Yakobo.
47. Kama 19 Solomo anammangira nyumba.
48. Komatu 20 Wamwambamwambayo sakhala m'nyumba zomangidwa ndi manja; monga mneneri anena,
49. 21 Thambo la kumwamba ndilo mpando wacifumu wanga,Ndi dziko lapansi copondapo mapazi anga:Mudzandimangira nyumba yotani? ati Ambuye;Kapena malo a mpumulo wanga ndi otani?
50. Silinapanga dzanja langa zinthu izi zonse kodi?