Macitidwe 7:38-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. 10 Uyu ndiye amene anali mu Mpingo m'cipululu pamodzi ndi mngelo wakulankhula naye m'phiri la Sina, ndi makolo athu: amene analandira maneno amoyo akutipatsa ife;

39. amene makolo athu sanafuna kumvera iye, koma anamkankha acoke, nabwerera m'mbuyo mumtima mwao ku Aigupto,

40. 11 nati ndi Aroni, Tipangireni milungu yotitsogoleraife; pakuti Mose uja, amene anatiturutsa m'Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

41. Ndipo 12 anapanga mwana wa ng'ombe masiku omwewo, nabwera nayo nsembe kwa fanolo, nasekerera ndi nchito za manja ao.

42. Koma 13 Mulungu anatembenuka, nawapereka iwo atumikire gulu la kumwamba; monga kwalembedwa m'buku laaneneri,14 Kodi mwapereka kwa Ine nyama zophedwa ndi nsembeZaka makumi anai m'cipululu, nyumba ya Israyeli inu?

Macitidwe 7