Macitidwe 5:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Koma Petro anati, Hananiya, Satana anadzaza mtima wako cifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wace wa mundawo?

4. Pamene unali nao, sunali wako kodi? ndipo pamene unaugulitsa sunali m'manja mwako kodi? bwanji cinalowa ici mumtima mwako? sunanyenga anthu, komatu Mulungu.

5. Koma Hananiya pakumva mau awa anagwa pansi namwalira: ndipo mantha akuru anagwera onse akumvawo.

6. Ndipo ananyamuka anyamata, namkulunga, namnyamula, naturuka naye, namuika.

Macitidwe 5