1. Koma munthu wina dzina lace Hananiya pamodzi ndi Safira mkazi wace,
2. anagulitsa cao, napatula pa mtengo wace, mkazi yemwe anadziwa, natenga cotsala, naciika pa mapazi a atumwi.
3. Koma Petro anati, Hananiya, Satana anadzaza mtima wako cifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wace wa mundawo?