Macitidwe 27:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo m'mene tidapita pang'ono pang'ono masiku ambiri, ndi kufika mobvutika pandunji pa Knido, ndipo popeza siinatilolanso mphepo, tinai pita m'tseri mwa Krete, pandunji pa Salimone;

8. ndipo popaza-pazapo mobvutika, tinafika ku malo ena dzina lace Pokoceza Pokoma; pafupi pamenepo panali mudzi wa Laseya.

9. Ndipo Itapita nthawi yambiri, ndipo unayambokhala woopsya ulendowo, popezanso nyengo ya kusala cakudya idapita kale, Paulo anawacenjeza,

Macitidwe 27