Macitidwe 27:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. ndipo m'mene adaukweza, anacita nazo zothandizira, nakulunga ngalawa; ndipo pakuopa kuti angatayike pa Surti, anatsitsa matanga, natengedwa motero.

18. Ndipo pobvutika kwakukuru ndi namondweyo, m'mawa mwace anayamba kutaya akatundu;

19. ndipo tsiku lacitatu anataya ndi manja ao a iwo eni zipangizo za ngalawa.

20. Ndipo m'mene dzuwa kapena nyenyezi sizinatiwalira masiku ambiri, ndipo namondwe wosati wamng'ono anatigwera, ciyembekezo conse cakuti tipulumuke cidaticokera pomwepo.

Macitidwe 27