Macitidwe 26:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Agripa anati kwa Paulo, Kwaloleka udzinenere wekha. Pamenepo Paulo, anatambasula dzanja nadzikanira:

2. Ndidziyesera wamwai, Mfumu Agripa, popeza nditi ndidzikanira lero pamaso panu, za zonse zimene Ayuda andinenera nazo;

3. makamaka popeza mudziwitsa miyambo yonse ndi mafunso onse a mwa Ayuda; cifukwa cace ndikupemphani mundimvere ine moleza mtima.

4. Mayendedwe a moyo wanga tsono, kuyambira pa cibwana canga, amene anakhala ciyambire mwa mtundu wanga m'Yerusalemu, awadziwa Ayuda onse;

Macitidwe 26