25. Ndipo m'mene anamfotokozera za cilungamo, ndi cidziletso, ndi ciweruziro cirinkudza, Felike anagwidwa ndi mantha, nayankha, Pita tsopano; ndipo ndikaona nthawi, ndidzakuitana iwe.
26. Anayembekezanso kuti Paulo adzampatsa ndalama; cifukwa cacenso anamuitana iye kawiri kawiri, nakamba naye.
27. Koma zitapita zaka ziwiri Porkiyo Festo analowa m'malo a Felike; ndipo Felike pofuna kukonda Ayuda anamsiya Paulo m'nsinga.