Macitidwe 22:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. anadza kwa ine, ndipo poimirirapo anati kwa ine, Saulo, mbale, penyanso. Ndipo ine, ora lomweli ndinampenya.

14. Ndipo anati, Mulungu wa makolo athu anakusankhiratu udziwe cifuniro cace, nuone Wolungamayo, numve mau oturuka m'kamwa mwace.

15. Ndipo udzamkhalira iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

16. Ndipo tsopano ucedweranji? Tauka, nubatizidwe ndi kusamba kucotsa macimo ako, nuitane pa dzina lace.

Macitidwe 22