33. Sindinasirira siliva, kapena golidi, kapena cobvala ca munthu ali yense.
34. Mudziwa inu nokha kuti manja anga awa anatumikira zosowa zanga, ndi za iwo akukhala ndi ine.
35. M'zinthu zonse ndinakupatsani citsanzo, cakuti pogwiritsa nchito, koteromuyenerakuthandiza ofoka ndi kukumbuka mau a Ambuye Yesu, kuti anati yekha, Kupatsa kutidalitsa koposa kulandira.
36. Ndipo m'mene ananena izi, anagwada pansi, napemphera ndi iwo onse.