Macitidwe 20:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo m'mene adakhalako miyezi itatu, ndipo a atampangira ciwembu Ayuda, pori iye apite ndi ngalawa ku Suriya, anatsimikiza mtima abwerere popyola Makedoniya.

4. Ndipo anamperekeza kufikira ku Asiya Sopatro mwana wa Puro, wa ku Bereya; ndipo Atesalonika, Aristarko ndi Sekundo; ndi Gayo wa ku Derbe, ndi Timoteo; ndi a ku Asiya, Tukiko ndi Trofimo.

5. Koma iwowa adatitsogolera, natilinda ku Trowa.

6. Ndipo tinapita m'ngalawa kucokera ku Filipi, atapita masiku a mkate wopanda cotupitsa, ndipo popita masiku asanu tinawapeza ku Trowa; pamenepo tinatsotsa masiku asanu ndi awiri.

Macitidwe 20