23. ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampacika ndi kumupha ndi manja a anthu osayeruzika;
24. yemweyo Mulungu anamuukitsa, atamasula zowawa za imfa, mwakuti sikunali kotheka kuti iye agwidwe nayo.
25. Pakuti Davine anena za Iye,Ndinaona Mbuye pamaso panga nthawi zonse;Cifukwa ali pa dzanja langa lamanja, kuti ndingasinthike;