Macitidwe 16:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. ndipo mwadzidzidzi panali cibvomezi cacikuru, cotero kuti maziko a ndende anagwedezeka: pomwepo pamakomo ponse panatseguka; ndi maunyolo a onse anamasuka.

27. Pamene anautsidwa kutulo mdindoyo, anaona kuti pa makomo a ndende panatseguka, ndipo anasolola lupanga lace, nati adziphe yekha, poyesa kuti am'ndende adathawa.

28. Koma Paulo anapfuula ndi mau akuru, nati, Usadzipweteka wekha; tonse tiri muno.

29. Ndipo mdindo anaitanitsa nyali, natumphira m'kati, alinkunthunthunrlra ndi mantha, nagwa pamaso pa Paulo ndi Sila,

Macitidwe 16