Macitidwe 15:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. ndipo sanalekanitsa ife ndi iwo, nayeretsa mitima yao m'cikhulupiriro.

10. Nanga bwanji tsopano mulikumuyesa Mulungu, kuti muike pa khosi la akuphunzira gori, limene sanatha kunyamula kapena makolo athu kapena ife?

11. Koma tikhulupira tidzapulumuka mwa cisomo ca Ambuye Yesu Kristu, monga iwo omwe.

12. Ndipo khamu lonse linatonthola; ndipo anamvera Bamaba ndi Paulo alikubwerezanso zizindikiro ndi zozizwitsa zimene Mulungu anacita nao pa amitundu.

13. Pamene iwo anatonthola Yakobo anayankha, nati,Abale, mverani ine:

Macitidwe 15