29. kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.
30. Tsono pamene iwo anamuka anatsikira ku Antiokeya; ndipo anasonkhanitsa khamu, napereka kalatayo.
31. Pamene anawerenga, anakondwera cifukwa ca cisangalatso cace.
32. Ndipo Yuda ndi Sila, okhala eni okha aneneri, anasangalatsa abale ndi mau ambiri, nawalimbikitsa.