12. Ndipo khamu lonse linatonthola; ndipo anamvera Bamaba ndi Paulo alikubwerezanso zizindikiro ndi zozizwitsa zimene Mulungu anacita nao pa amitundu.
13. Pamene iwo anatonthola Yakobo anayankha, nati,Abale, mverani ine:
14. Sumeoni wabwereza kuti poyamba Mulungu anayang'anira amitundu, kuti atenge mwa iwo anthu a dzina lace.
15. Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,
16. Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa;Ndidzamanganso zopasuka zace,Ndipo ndidzaciimikanso:
17. Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,
18. Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.