Macitidwe 13:28-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo ngakhale sanapeza cifukwa ca kumphera, anapempha Pilato kuti aphedwe.

29. Ndipo atatsiriza zonse zolembedwa za iye, anamtsitsa kumtengo, namuika m'manda.

30. Koma Mulungu anamuukitsa iye kwa akufa;

31. ndipo 1 anaonekera masiku ambiri ndi iwo amene anamperekeza iye pokwera ku Yerusalemu kucokera ku Galileya, amenewo ndiwo akumcitira umboni tsopano kwa anthu.

32. Ndipo ife tikulalikirani inu Uthenga Wabwino wa 2 lonjezano locitidwa kwa makolo;

33. kuti Mulungu analikwaniritsa ili kwa ana athu pakuukitsa Yesu; monganso mulembedwa m'Salmo laciwiri, Iwe ndiwe Mwana wanga, lero ndakubala.

Macitidwe 13