Macitidwe 11:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma panali ena mwa iwo, amuna a ku Kupro, ndi Kurene, amenewo, m'mene adafika ku Antiokeya, analankhula ndi Ahelene, ndi kulalikira Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.

21. Ndipo dzanja la Ambuye linali nao; ndi unyinji wakukhulupira unatembenukira kwa Ambuye.

22. Ndipo mbiri yao inamveka m'makutu a Mpingo wakukhala m'Yerusalemu; ndipo anatuma Bamaba apite kufikira ku Antiokeya;

23. ameneyo, m'mene anafika, naona cisomo ca Mulungu, anakondwa; ndipo anawandandaulira onse, kuti atsimikize mtima kukhalabe ndi Ambuye;

Macitidwe 11