1. Koma atumwi ndi abale akukhala m'Yudeya anamva kuti amitundunso adalandira mau a Mulungu.
2. Ndipo pamene Petro adakwera kudza ku Yerusalemu, iwo a kumdulidwe anatsutsana naye,
3. nanena kuti, Munalowa kwa anthu osadulidwa, ndi kudya nao.
4. Koma Petro anayamba kuwafotokozera cilongosolere, nanena,