Macitidwe 10:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. koma m'mene analikumkonzera cakudya kudamgwera ngati kukomoka;

11. ndipo anaona pathambo padatseguka, ndi cotengera cirinkutsika, conga ngati cinsaru cacikuru, cogwiridwa pa ngondya zace zinai, ndi kutsikira padziko pansi;

12. m'menemo munali nyama za miyendo inai za mitundu yonse, ndi zokwawa za padziko ndi mbalame za m'mlengalenga.

Macitidwe 10