Luka 9:46-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Ndipo anayamba kutsutsana kuti wamkulu mwa iwo ndani.

47. Koma Yesu pakuona kutsutsana kwa mitima yao, anatenga kamwana, nakaimika pambali pace, nati kwa iwo,

48. Amene ali yense akalandire kamwana aka m'dzina langa alandira Ine; ndipo amene andilandira Ine alandira iye amene anandituma Ine; pakuti iye wakukhala wamng'onong'ono wa inu nonse, yemweyu ndiye wamkuru.

Luka 9