17. Pakuti palibe cinthu cobisika, cimene sicidzakhala coonekera; kapena cinsinsi cimene sicidzadziwika ndi kubvumbuluka.
18. Cifukwa cace yang'anirani mamvedwe anu; pakuti kudzapatsidwa kwa iye amene ali naco; ndipo kwa iye amene alibe cidzacotsedwa, cingakhale cija aoneka ngati ali naco.
19. Ndipo anadza kwa iye amace ndi abale ace, ndipo sanakhoza ku: mfika, cifukwa ca khamu la anthu.
20. Ndipo anamuuza iye, kuti, Amai wanu ndi abale anu alinkuima kunja, nafuna kuona Inu.