Luka 24:40-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.

41. Koma pokhala iwo cikhalire osakhulupirira cifukwa ca cimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, 3 Muli nako kanthu kakudya kuno?

42. Ndipo anampatsa iye cidutsu ca nsomba yokazinga.

43. Ndipo 4 anacitenga, nacidya pamaso pao.

44. Ndipo anati kwa iwo, 5 Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'cilamulo ca 6 Mose, ndi aneneri, ndi masalmo.

45. Ndipo 7 anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;

46. ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;

47. ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi 9 kukhululukidwa kwa macimo kwa 10 mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.

Luka 24