Luka 23:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo m'mene anadziwa kuti ali wa m'ulamuliro wace wa Herode, anamtumiza iye kwa Herode, amene anali iye mwini ku Yerusalemu masiku awa,

8. Ndipo Herode, pamene anaona Yesu, anakondwa ndithu; pakuti anayamba kale kufuna kumpenya iye, cifukwa anamva za iye; nayembekeza kuona cizindikilo cina cocitidwa ndi iye.

9. Ndipo anamfunsa iye mau ambiri; koma iye sanamyankha kanthu.

Luka 23