Luka 23:53-56 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

53. Ndipo 4 anautsitsa, naukulunga m'nsaru yabafuta, nauika m'manda osemedwa m'mwala, m'menemo sanaika munthu ndi kale lonse.

54. Ndipo panali tsiku lokonzera, ndi Sabata linayandikira.

55. Ndipo 5 akazi, amene anacokera naye ku Galileya, anatsata m'mbuyo, naona manda, ndi maikidwe a mtembo wace.

56. Ndipo anapita kwao, 6 nakonza zonunkhira ndi mafuta abwino. Ndipo pa Sabata anapumula 7 monga mwa lamulo.

Luka 23