Luka 22:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. ndipo Ine ndikuikirani ufumu, monganso Atate wanga anandiikira Ine, kuti mukadye ndi kumwa kugome kwanga mu Ufumu wanga;

30. ndipo mudzakhala pa mipando yacifumu ndi kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

31. Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu;

32. koma ndinakupempherera kuti cikhulupiriro cako cingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

33. Ndipo anati kwa iye, Ambuye, ndiripo ndikapite ndi Inu kundende ndikuimfa.

Luka 22