Luka 21:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. anthu akukomoka ndi mantha, ndi kuyembekeeera zinthu zirinkudza ku dziko lapansi;

27. pakuti mphamvu zakumwamba zidzagwedezeka. Ndipo pamenepo adzaona Mwana wa munthu alinkudza mu mtambo ndi mphamvu ndi ulemerero waukuru.

28. Komapoyamba kucitika izi weramukani, tukulani mitu yanu; cifukwa ciomboledwe canu cayandikira.

29. Ndipo ananena nao fanizo; Onani mkuyu, ndi mitengo yonse:

30. pamene iphukira, muipenya nimuzindikira pa nokha kuti dzinja liri pafupi pomwepo.

31. Inde cotero inunso, pakuona zinthu izi zirikucitika, zindikirani kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi.

Luka 21