15. Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.
16. Koma mudzaperekedwa ngakhale ndi akukubalani, ndi abale, ndi a pfuko lanu, ndi abwenzi anu; ndipo ena a inu adzakuphani,
17. Ndipo anthu onse adzadana ndi inu cifukwa ca dzina langa.
18. Ndipo silidzaonongeka tsitsi limodzi la pamutu panu.
19. Mudzakhala nao moyo wanu m'cipiriro.