Luka 21:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.

16. Koma mudzaperekedwa ngakhale ndi akukubalani, ndi abale, ndi a pfuko lanu, ndi abwenzi anu; ndipo ena a inu adzakuphani,

17. Ndipo anthu onse adzadana ndi inu cifukwa ca dzina langa.

18. Ndipo silidzaonongeka tsitsi limodzi la pamutu panu.

19. Mudzakhala nao moyo wanu m'cipiriro.

Luka 21