Luka 18:32-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Pakuti adzampereka kwa amitundu, nadzamseka, nadzamcitira cipongwe, nadzamthira malobvu; ndipo atamkwapula adzamupha iye;

33. ndipo tsiku lacitatu adzauka.

34. Ndipo sanadziwitsa kanthu ka izi; ndi mau awa adawabisikira, ndipo sanazindikira zonenedwazo.

35. Ndipo kunali, pamene anayandikira ku Yeriko, msaona wina anakhala m'mbali mwa njira, napemphapempha;

36. ndipo pakumva khamu la anthu alinkupita, anafunsa, ici nciani?

37. Ndipo anamuuza iye, kuti, Yesu Mnazarayo alinkupita.

38. Ndipo anapfuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davine, mundicitire cifundo.

Luka 18