Luka 18:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Udziwa malamulo. Usacite cigololo, Usaphe, Usabe, Usacite umboni wonama, Lemekeza atate wako ndi amako.

21. Koma anati, Izi zonse ndazisunga kuyambira ubwana wanga.

22. Koma m'mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa cinthu cimodzi: gulitsa ziri zonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala naco cuma ceni ceni m'Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

23. Koma pakumva izi anagwidwa naco cisoni cambiri; pakuti anali mwini cuma cambiri.

Luka 18