Luka 17:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo monga kunakhala masiku a Nowa, momwemo kudzakhalanso masiku a Mwana wa munthu.

27. Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m'cingalawa, ndipo cinadza cigumula, niciwaononga onsewo.

28. Monga momwenso kunakhala masiku a Loti; anadya, anamwa, anagula, anagulitsa, anabzala, anamanga nyumba;

29. koma tsiku limene Loti anaturuka m'Sodoma udabvumba mota ndi sulfure zocokera kumwamba, ndipo zinawaononga onsewo;

30. momwemo kudzakhala tsiku lakubvumbuluka Mwana wa munthu.

Luka 17