Luka 16:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma Abrahamu anati, Mwana, kumbukila kuti unalandira zokoma zako pakukhala m'moyo iwe, momwemonso Lazaro zoipa; ndipo tsopano iye asangalatsidwa pano, koma iwe uzunzidwadi.

26. Ndipo pamwamba pa izi, pakati pa ife ndi inu pakhazikika phompho lalikuru, kotero kuti iwo akufuna kuoloka kucokera kuno kunka kwa inu sangathe, kapena kucokera kwanuko kuyambuka kudza kwa ife, sangathenso.

27. Koma anati, Pamenepo ndikupemphani, Atate, kuti mumtume ku nyumba ya atate wanga;

28. pakuti ndirinao abale asanu; awacitire umboni iwo kuti iwonso angadze ku malo ana a mazunzo.

29. Koma Abrahamu anati, Ali ndi Mose ndi aneneri; amvere iwo.

Luka 16