Luka 12:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Kotero ngati simungathe ngakhale cacing'onong'ono, muderanji nkhawa cifukwa ca zina zija?

27. Lingalirani maluwa, makulidwe ao; sagwiritsa nchito ndi kusapota; koma ndinena kwa inu, Ngakhale Solomo, mu ulemerero wace wonse, sanabvala ngati limodzi la awa.

28. Koma ngati Mulungu abveka kotere maudzu a kuthengo akukhala lero, ndipo mawa aponyedwa pamoto; nanga inu sadzakuninkhani koposa, inu okhulupirira pang'ono?

29. Ndipo inu musafunefune cimene mudzadya, ndi cimene mudzamwa; ndipo musakayike mtima.

Luka 12