Luka 10:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo anati kwa iye, M'cilamulo mulembedwa ciani? Uwerenga bwanji?

27. Ndipo iye anayankha nati, 3 Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

28. Ndipo anati kwa iye, Wayankha bwino; cita ici, ndipo udzakhala ndi moyo.

29. Koma iye, pofuna kudziyesa yekha wolungama, anati kwa Yesu, Ndipo mnansi wanga ndani?

Luka 10