Luka 10:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Lingakhale pfumbi locokera kumudzi kwanu, lomamatika ku mapaziathu, tilisansira pa inu; koma zindikirani ici, kuti Ufumu wa Mulungu wayandikira.

12. Ndinena ndi inu kuti tsiku lijalo ku Sodoma kudzapiririka kuposa mudzi umenewo.

13. Tsoka iwe, Korazini! tsoka iwe Betsaida! cifukwa kuti zikadacitika m'Turo ndi Sidoni zamphamvuzi zidacitika mwa inu, akadalapa kale lomwe ndi kukhala pansi obvala ciguduli ndi phulusa.

14. Koma ku Turo ndi Sidoni kudzapiririka m'ciweruziro, koposa inu.

Luka 10