Luka 1:47-53 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. Ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

48. Cifukwa iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wace;Pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzandichula ine wodala.

49. Cifukwa iye Wamphamvuyo anandicitira ine zazikuru;4 Ndipo dzina lace liri loyera.

50. 5 Ndipo cifundo cace cifikira anthu a mibadwo mibadwoPa iwo amene amuopa iye.

51. Iye anacita zamphamvu ndi mkono wace;6 Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao,

52. iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu,Ndipo anakweza aumphawi,

53. 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino,Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.

Luka 1