19. ndi a nkhosa, ndi mcira wamafuta, ndi cophimba matumbo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa;
20. ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.
21. Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.
22. Ndipo Aroni anakweza dzanja lace kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.