2. Tenga Aroni ndi ana ace pamodzi naye ndi zobvalazo, ndi mafuta odzozawo, ndi ng'ombe ya nsembe yaucimoyo, ndi nkhosa zamphongo ziwirizo, ndi mtanga wa mkate wopanda cotupitsawo;
3. nusonkhanitse khamu lonse ku khomo la cihema cokomanako.
4. Ndipo Mose anacita monga Yehova anamuuza; ndi khamulo linasonkhana pa khomo la cihema cokomanako.
5. Ndipo Mose anati kwa msonkhanowo, Ici ndi cimene Yehova adauza kuti cicitike.