8. Ndipo acotse mafuta onse a ng'ombe ya nsembe yaucimo, acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
9. ndi imso ziwiri ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso,
10. umo azikacotsera pa ng'ombe ya nsembe yoyamika; ndipo wansembe azitenthe pa guwa la nsembe yopsereza.
11. Naturutse cikopa ca ng'ombeyo, ndi nyama yace yonse, pamodzi ndi mutu wace, ndi miyendo yace, ndi matumbo ace, ndi cipwidza cace,
12. inde ng'ombe yonse, kunja kwa cigono, kumka nayo kumalo koyera, kumene atayako mapulusa, naitenthe pankhuni ndi moto; aitenthe potayira mapulusa.