Levitiko 23:41-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo muwasunge madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri m'caka; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; musunge mwezi wacisanu ndi ciwiri.

42. Mukhale m'misasa masiku asanu ndi awiri; onse obadwa m'dziko mwa Israyeli akhale m'misasa;

43. kuti mibadwo yanu ikadziwe lruti ndinakhalitsa ana a Israyeli m'misasa, pamene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

44. Ndipo Mose anafotokozera ana a Israyeli nyengo zoikika za Yehova.

Levitiko 23