Levitiko 22:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti, Zikamabadwa ng'ombe kapena nkhosa, kapena mbuzi, zikhale ndi mace masiku asanu ndi awiri;

27. kuyambira tsiku lacisanu ndi citatu ndi m'tsogolo mwace, idzalandirika ngati copereka nsembe yamoto ya Yehova.

28. Koma musamaipha ng'ombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wace tsiku limodzimodzi.

29. Ndipo mukamaphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandirike.

30. Idyedwe tsiku lomwelo; musamasiyako kufikira m'mawa; Ine ndine Yehova.

Levitiko 22